< Masalimo 17 >

1 Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
Psalm: Oratio David. Exaudi Domine iustitiam meam: intende deprecationem meam. Auribus percipe orationem meam, non in labiis dolosis.
2 Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
De vultu tuo iudicium meum prodeat: oculi tui videant aequitates.
3 Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Probasti cor meum, et visitasti nocte: igne me examinasti, et non est inventa in me iniquitas.
4 Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
Ut non loquatur os meum opera hominum: propter verba labiorum tuorum ego custodivi vias duras.
5 Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
Perfice gressus meos in semitis tuis: ut non moveantur vestigia mea.
6 Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
Ego clamavi, quoniam exaudisti me Deus: inclina aurem tuam mihi, et exaudi verba mea.
7 Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Mirifica misericordias tuas, qui salvos facis sperantes in te.
8 Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
A resistentibus dexterae tuae custodi me, ut pupillam oculi. Sub umbra alarum tuarum protege me:
9 kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
a facie impiorum qui me afflixerunt. Inimici mei animam meam circumdederunt,
10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
adipem suum concluserunt: os eorum locutum est superbiam.
11 Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
Proiicientes me nunc circumdederunt me: oculos suos statuerunt declinare in terram.
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
Susceperunt me sicut leo paratus ad praedam: et sic catulus leonis habitans in abditis.
13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
Exurge Domine, praeveni eum, et supplanta eum: eripe animam meam ab impio, frameam tuam
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
ab inimicis manus tuae. Domine a paucis de terra divide eos in vita eorum: de absconditis tuis adimpletus est venter eorum. Saturati sunt filiis: et dimiserunt reliquias suas parvulis suis.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.
Ego autem in iustitia apparebo conspectui tuo: satiabor cum apparuerit gloria tua.

< Masalimo 17 >