< Masalimo 17 >

1 Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
Prière de David.
2 Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
Que de vous émane mon jugement; que vos yeux voient l’équité.
3 Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Vous avez éprouvé mon cœur, et vous l’avez visité pendant la nuit; vous m’avez exaucé en me faisant passer par le feu, et il ne s’est pas trouvé en moi d’iniquité.
4 Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
Afin que ma bouche ne parle pas même des œuvres des hommes, j’ai gardé, à cause des paroles de vos lèvres, des voies dures.
5 Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
Affermissez mes pas dans vos sentiers, afin que mes pieds ne soient point ébranlés.
6 Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
Moi, j’ai crié, parce que vous m’avez exaucé, mon Dieu; inclinez votre oreille vers moi, et exaucez mes paroles.
7 Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Faites éclater vos miséricordes, vous qui sauvez ceux qui espèrent en vous.
8 Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
Contre ceux qui résistent à votre droite, gardez-moi comme la prunelle de l’œil. Sous l’ombre de vos ailes, protégez-moi,
9 kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
Contre la face des impies qui m’ont tourmenté. Mes ennemis ont environné mon âme,
10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
Ils ont fermé leurs entrailles, leur bouche a parlé orgueil,
11 Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
Après m’avoir rejeté, maintenant ils m’environnent, ils ont résolu d’incliner leurs yeux vers la terre.
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
Ils m’ont saisi comme un lion préparé pour la proie, et comme le petit d’un lion qui habite dans des lieux cachés.
13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
Levez-vous, Seigneur, prévenez-le et renversez-le, arrachez mon âme à l’impie, votre épée à double tranchant
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
Aux ennemis de votre main. Seigneur, séparez-les pendant leur vie du petit nombre de ceux qui sont à vous sur la terre; leur sein est rempli de vos biens cachés. Ils sont rassasiés d’enfants, et ils laissent le reste de leurs biens à leurs petits-enfants.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.
Mais moi, dans ma justice, j’apparaîtrai en votre présence; je serai rassasié lorsque votre gloire m’aura apparu.

< Masalimo 17 >