< Masalimo 17 >

1 Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
Prière de David. Éternel, écoute ma juste cause! Sois attentif à mon cri! Prête l'oreille à ma prière: elle sort de lèvres sans fraude!
2 Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
Que ta présence fasse éclater mon droit; Que tes yeux reconnaissent mon intégrité!
3 Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Tu as sondé mon coeur, tu m'as visité pendant la nuit; Tu m'as éprouvé, tu ne trouves rien; Ma parole ne va pas au-delà de ma pensée.
4 Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
J'ai vu les actions des hommes; Mais, pour obéir à la parole de ta bouche. Je me suis éloigné des voies de l'homme violent.
5 Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
Affermis mes pas dans tes sentiers, Afin que mes pieds ne chancellent point.
6 Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
Je t'invoque; car tu m'exauces, ô Dieu! Incline ton oreille vers moi; écoute ma prière!
7 Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Fais-nous admirer tes bontés, Toi qui sauves ceux qui cherchent leur refuge Auprès de toi, contre leurs adversaires!
8 Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
Garde-moi comme la prunelle de l'oeil! Cache-moi à l'ombre de tes ailes,
9 kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
Loin de ces méchants qui m'oppriment, De mes ennemis acharnés qui m'enveloppent!
10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
Ils ferment leur coeur à la pitié; Leur bouche tient des discours hautains.
11 Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
A chaque pas, ils nous circonviennent; Ils nous épient pour nous terrasser.
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
Ils ressemblent au lion avide de déchirer. Au lionceau qui se tient aux aguets dans son repaire.
13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
Lève-toi, ô Éternel! Marche à la rencontre du méchant; renverse-le! Que ton épée me délivre de lui!
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
Que ta main, ô Éternel, me délivre de ces hommes, Des hommes de ce siècle, Dont tout le bonheur est dans cette vie, Et dont le ventre est gorgé de tes biens: Leurs enfants ont tout à satiété, Et ils laissent encore leur superflu à leurs petits-enfants.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.
Mais moi, grâce à ma droiture, je pourrai voir ta face. A mon réveil, je me rassasierai de ta vue.

< Masalimo 17 >