< Masalimo 17 >

1 Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
Prière de David. Ecoute, ô Seigneur, ma juste demande, exauce ma supplication, prête l’oreille à ma prière, sortant de lèvres non trompeuses.
2 Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
C’Est de toi qu’émanera mon bon droit: tes yeux discernent ce qui est équitable.
3 Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Tu sondes mon cœur, tu m’examines pendant la nuit, tu me mets à l’épreuve, sans trouver en moi aucune pensée qui ne doive passer par ma bouche.
4 Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
Guidé par les paroles de tes lèvres, j’observe les actions des hommes, les voies des gens violents.
5 Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
Affermis mes pas dans tes sentiers, pour que mes pieds ne glissent point.
6 Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
Je t’appelle, car tu me réponds, ô Dieu! Prête-moi l’oreille, entends mes paroles.
7 Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Mets en relief tes bienfaits, ô Protecteur de ceux qui se confient à ta droite, malgré les adversaires.
8 Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
Garde-moi comme la prunelle des yeux, abrite-moi à l’ombre de tes ailes,
9 kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
contre les méchants qui me tyrannisent, contre mes ennemis qui me cernent avec passion.
10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
De leur graisse ils ont bouché leur cœur; leurs lèvres s’expriment avec orgueil.
11 Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
A chacun de nos pas, les voilà qui se pressent autour de nous; ils ont les yeux sur nous pour nous étendre à terre,
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
pareils au lion avide de déchirer, au lionceau qui se tient en embuscade.
13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
Lève-toi, Seigneur, préviens ses desseins, fais-lui ployer le genou; par ton glaive, sauve ma vie du méchant.
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
Par ta main, ô Eternel, sauve-moi de ces gens, de ces gens esclaves du monde, qui jouissent largement de la vie, dont tu bourres le ventre de tes biens, dont les enfants ont tout en abondance et laissent leur superflu à leur progéniture.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.
Quant à moi, puissé-je, grâce à ma droiture, contempler ta face et, à mon réveil, me rassasier de ta vue!

< Masalimo 17 >