< Masalimo 17 >

1 Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
[A Prayer by David.] Hear, LORD, my righteous plea; Give ear to my prayer, that doesn't go out of deceitful lips.
2 Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
Let my sentence come forth from your presence. Let your eyes look on equity.
3 Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
You have proved my heart. You have visited me in the night. You have tried me, and found nothing. I have resolved that my mouth shall not disobey.
4 Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
As for the works of men, by the word of your lips, I have kept myself from the ways of the violent.
5 Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
My steps have held fast to your paths. My feet have not slipped.
6 Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
I have called on you, for you will answer me, God. Turn your ear to me. Hear my speech.
7 Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Show your marvelous loving kindness, you who save those who take refuge by your right hand from their enemies.
8 Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
Keep me as the apple of your eye. Hide me under the shadow of your wings,
9 kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
from the wicked who oppress me, my deadly enemies, who surround me.
10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
They close up their callous hearts. With their mouth they speak proudly.
11 Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
They have tracked me down; suddenly they surround me. They watch closely, crouching down to the ground.
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
He is like a lion that is greedy of his prey, as it were a young lion lurking in secret places.
13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
Arise, LORD, confront him. Cast him down. Deliver my soul from the wicked by your sword;
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
from men with your hand, LORD, from men of the world, whose portion is in this life. You fill their womb with treasure. They are satisfied with children, and they leave their wealth to their little ones.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.
As for me, I shall see your face in righteousness. I shall be satisfied, when I awake, with seeing your form.

< Masalimo 17 >