< Masalimo 17 >

1 Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
A Prayer of David. Hear the right, O LORD, attend unto my cry, give ear unto my prayer, [that goeth] not out of feigned lips.
2 Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
Let my sentence come forth from thy presence; let thine eyes behold the things that are equal.
3 Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Thou hast proved mine heart; thou hast visited [me] in the night; thou hast tried me, [and] shalt find nothing; I am purposed [that] my mouth shall not transgress.
4 Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
Concerning the works of men, by the word of thy lips I have kept [me from] the paths of the destroyer.
5 Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
Hold up my goings in thy paths, [that] my footsteps slip not.
6 Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
I have called upon thee, for thou wilt hear me, O God: incline thine ear unto me, [ and hear] my speech.
7 Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Shew thy marvellous lovingkindness, O thou that savest by thy right hand them which put their trust [in thee] from those that rise up [against them].
8 Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
Keep me as the apple of the eye, hide me under the shadow of thy wings,
9 kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
From the wicked that oppress me, [from] my deadly enemies, [who] compass me about.
10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
They are inclosed in their own fat: with their mouth they speak proudly.
11 Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
They have now compassed us in our steps: they have set their eyes bowing down to the earth;
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
Like as a lion [that] is greedy of his prey, and as it were a young lion lurking in secret places.
13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
Arise, O LORD, disappoint him, cast him down: deliver my soul from the wicked, [which is] thy sword:
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
From men [which are] thy hand, O LORD, from men of the world, [which have] their portion in [this] life, and whose belly thou fillest with thy hid [treasure: ] they are full of children, and leave the rest of their [substance] to their babes.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.
As for me, I will behold thy face in righteousness: I shall be satisfied, when I awake, with thy likeness.

< Masalimo 17 >