< Masalimo 17 >
1 Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
(En bøn af David.) HERRE, hør en retfærdig Sag, lyt til min Klage lån Øre til Bøn fra svigløse Læber!
2 Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
Fra dig skal min Ret udgå, thi hvad ret er, ser dine Øjne.
3 Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Prøv mit Hjerte, se efter om Natten, ransag mig, du finder ej Svig hos mig.
4 Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
Ej synded min Mund, hvad end Mennesker gjorde; ved dine Læbers Ord vogted jeg mig for Voldsmænds Veje;
5 Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
mine Skridt har holdt dine Spor, jeg vaklede ej på min Gang.
6 Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
Jeg råber til dig, thi du svarer mig, Gud, bøj Øret til mig, hør på mit Ord!
7 Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Vis, dig underfuldt nådig, du Frelser for dem, der tyr til din højre for Fjender!
8 Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
Vogt mig som Øjestenen, skjul mig i dine Vingers Skygge
9 kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
for gudløse, der øver Vold imod mig, glubske Fjender, som omringer mig;
10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
de har lukket deres Hjerte med Fedt, deres Mund fører Hovmodstale.
11 Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
De omringer os, overalt hvor vi går, de sigter på at slå os til Jorden.
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
De er som den rovgridske Løve, den unge Løve, der ligger på Lur.
13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
Rejs dig, HERRE, træd ham i Møde, kast ham til Jorden, fri med dit Sværd min Sjæl fra den gudløses Vold,
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
fra Mændene, HERRE, med din Hånd, fra dødelige Mænd - lad dem få deres Del i levende Live! Fyld deres Bug med dit Forråd af Vrede, lad Børnene mættes dermed og efterlade deres Børn, hvad de levner!
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.
Men jeg skal i Retfærd skue dit Åsyn, mættes ved din Skikkelse, når jeg vågner.