< Masalimo 16 >

1 Mikitamu ya Davide. Ndisungeni Inu Mulungu, pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
Psalmus David. Conserva me Domine, quoniam speravi in te.
2 Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga; popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
Dixi Domino: Deus meus es tu, quoniam bonorum meorum non eges.
3 Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
Sanctis, qui sunt in terra eius, mirificavit omnes voluntates meas in eis.
4 Anthu amene amathamangira kwa milungu ina mavuto awo adzachulukadi. Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
Multiplicatae sunt infirmitates eorum: postea acceleraverunt. Non congregabo conventicula eorum de sanguinibus: nec memor ero nominum eorum per labia mea.
5 Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa; mwateteza kolimba gawo langa.
Dominus pars hereditatis meae, et calicis mei: tu es, qui restitues hereditatem meam mihi.
6 Malire a malo anga akhala pabwino; ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
Funes ceciderunt mihi in praeclaris: etenim hereditas mea praeclara est mihi.
7 Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu; ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
Benedicam Dominum, qui tribuit mihi intellectum: insuper et usque ad noctem increpuerunt me renes mei.
8 Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
Providebam Dominum in conspectu meo semper: quoniam a dextris est mihi, ne commovear.
9 Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
Propter hoc laetatum est cor meum, et exultavit lingua mea: insuper et caro mea requiescet in spe.
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol h7585)
Quoniam non derelinques animam meam in inferno: nec dabis sanctum tuum videre corruptionem. (Sheol h7585)
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo; mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu, ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.
Notas mihi fecisti vias vitae, adimplebis me laetitia cum vultu tuo: delectationes in dextera tua usque in finem.

< Masalimo 16 >