< Masalimo 16 >
1 Mikitamu ya Davide. Ndisungeni Inu Mulungu, pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
Michtham Davids. Behüte mich, Gott, denn ich verlasse mich auf Dich.
2 Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga; popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
Ich spreche zu Jehovah: Du bist mein Herr, mein Gutes reicht nicht an Dich.
3 Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
An den Heiligen, die im Lande sind, und an den Herrlichen, an ihnen habe ich all meine Lust.
4 Anthu amene amathamangira kwa milungu ina mavuto awo adzachulukadi. Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
Sie mehren ihre Schmerzen, einem anderen eilen sie nach. Nicht gieße ich ihre Trankopfer von Blut, und trage ihre Namen nicht auf meinen Lippen.
5 Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa; mwateteza kolimba gawo langa.
Jehovah, mein Anteil bist Du am Teile und mein Becher; Du erhältst mein Los.
6 Malire a malo anga akhala pabwino; ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
Mein Los ist mir aufs Lieblichste gefallen, ja, mein Erbe ist hold.
7 Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu; ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
Jehovah segne ich, Der mich beraten hat, ja, in den Nächten züchtigen mich meine Nieren.
8 Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
Jehovah habe ich beständig vor mich gestellt. Weil Er mir zur Rechten ist, wanke ich nicht.
9 Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
Darum ist fröhlich mein Herz, und frohlockt meine Herrlichkeit; ja, mein Fleisch wohnt in Sicherheit.
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol )
Denn nicht läßt Du in der Hölle meine Seele, Deinen Heiligen gibst Du nicht hin, die Verwesung zu sehen. (Sheol )
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo; mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu, ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.
Du machst kund mir des Lebens Pfad, Fülle der Fröhlichkeit ist vor Deinem Angesicht, Lieblichkeit in Deiner Rechten immerdar.