< Masalimo 16 >
1 Mikitamu ya Davide. Ndisungeni Inu Mulungu, pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
Mitcam (cantique) de David. Garde-moi, ô Dieu! car je me suis retiré vers toi.
2 Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga; popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
J'ai dit à l'Éternel: Tu es le Seigneur, je n'ai point de bien au-dessus de toi.
3 Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
C'est dans les saints, et dans les nobles âmes qui sont sur la terre, que je prends tout mon plaisir.
4 Anthu amene amathamangira kwa milungu ina mavuto awo adzachulukadi. Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
Les idoles des impies se multiplient, ils courent après d'autres dieux: je ne ferai pas leurs aspersions de sang, et leur nom ne passera point par ma bouche.
5 Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa; mwateteza kolimba gawo langa.
L'Éternel est mon héritage et ma portion; c'est toi qui m'assures mon lot.
6 Malire a malo anga akhala pabwino; ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
Ma possession m'est échue dans des lieux agréables, et un très bel héritage m'est échu.
7 Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu; ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
Je bénirai l'Éternel qui est mon conseil; les nuits même mon cœur m'instruit au-dedans de moi.
8 Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
J'ai eu l'Éternel constamment présent devant moi; puisqu'il est à ma droite, je ne serai point ébranlé.
9 Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
C'est pourquoi mon cœur se réjouit, et mon âme chante de joie; et ma chair même reposera en assurance.
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol )
Car tu n'abandonneras pas mon âme au Sépulcre; tu ne permettras point que ton saint voie la corruption. (Sheol )
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo; mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu, ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.
Tu me feras connaître le chemin de la vie; il y a un rassasiement de joie devant ta face, et des délices à ta droite pour jamais.