< Masalimo 16 >
1 Mikitamu ya Davide. Ndisungeni Inu Mulungu, pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
The inscription of a title to David himself. Preserve me, O Lord, for I have put trust in thee.
2 Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga; popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
I have said to the Lord, thou art my God, for thou hast no need of my goods.
3 Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
To the saints, who are in his land, he hath made wonderful all my desires in them.
4 Anthu amene amathamangira kwa milungu ina mavuto awo adzachulukadi. Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
Their infirmities were multiplied: afterwards they made haste. I will not gather together their meetings for blood offerings: nor will I be mindful of their names by my lips.
5 Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa; mwateteza kolimba gawo langa.
The Lord is the portion of my inheritance and of my cup: it is thou that wilt restore my inheritance to me.
6 Malire a malo anga akhala pabwino; ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
The lines are fallen unto me in goodly places: for my inheritance is goodly to me.
7 Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu; ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
I will bless the Lord, who hath given me understanding: moreover my reins also have corrected me even till night.
8 Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
I set the Lord always in my sight: for he is at my right hand, that I be not moved.
9 Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
Therefore my heart hath been glad, and my tongue hath rejoiced: moreover my flesh also shall rest in hope.
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol )
Because thou wilt not leave my soul in hell; nor wilt then give thy holy one to see corruption. (Sheol )
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo; mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu, ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.
Thou hast made known to me the ways of life, thou shalt fill me with joy with thy countenance: at thy right hand are delights even to the end.