< Masalimo 150 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
هللویاه! خدا را در قدس او تسبیح بخوانید. در فلک قوت او، او راتسبیح بخوانید!۱
2 Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
او را به‌سبب کارهای عظیم اوتسبیح بخوانید. او را به حسب کثرت عظمتش تسبیح بخوانید.۲
3 Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
او را به آواز کرنا تسبیح بخوانید. او را با بربط و عود تسبیح بخوانید.۳
4 Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
اورا با دف و رقص تسبیح بخوانید. او را با ذوات اوتار و نی تسبیح بخوانید.۴
5 Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
او را با صنجهای بلندآواز تسبیح بخوانید. او را با صنجهای خوش صدا تسبیح بخوانید.۵
6 Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.
هرکه روح دارد، خداوند را تسبیح بخواند. هللویاه!۶

< Masalimo 150 >