< Masalimo 150 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
Lobet Jah! / Lobt El in seinem Heiligtum, / Lobt ihn an seiner mächtigen Feste!
2 Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
Lobt ihn ob seiner gewaltigen Taten, / Lobt ihn, wie es seiner überschwenglichen Größe geziemt!
3 Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
Lobt ihn mit dem Blasen des Widderhorns, / Lobt ihn mit Harfe und Zither!
4 Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
Lobt ihn mit Pauke und Reigen, / Lobt ihn mit Saitenspiel und Flöte!
5 Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
Lobt ihn mit klingenden Zimbeln, / Lobt ihn mit schallenden Zimbeln!
6 Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.
Alles, was Oden hat, lobe Jah! / Lobet Jah!

< Masalimo 150 >