< Masalimo 150 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
Praise the LORD. Praise God in his sanctuary. Praise him in his heavens for his acts of power.
2 Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
Praise him for his mighty acts. Praise him according to his excellent greatness.
3 Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
Praise him with the sounding of the trumpet. Praise him with harp and lyre.
4 Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
Praise him with tambourine and dancing. Praise him with stringed instruments and flute.
5 Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
Praise him with loud cymbals. Praise him with resounding cymbals.
6 Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.
Let everything that has breath praise the LORD. Praise the LORD.

< Masalimo 150 >