< Masalimo 150 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
Hallelujah! Praise God in his sanctuary; praise him in the firmament of his power.
2 Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
Praise him in his mighty acts; praise him according to the abundance of his greatness.
3 Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
Praise him with the sound of the trumpet; praise him with lute and harp;
4 Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
Praise him with the tambour and dance; praise him with stringed instruments and the pipe;
5 Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
Praise him with loud cymbals; praise him with high sounding cymbals.
6 Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.
Let everything that hath breath praise Jah. Hallelujah!

< Masalimo 150 >