< Masalimo 150 >
1 Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
Alleluia. Praise God in his holy places: praise him in the firmament of his power.
2 Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
Praise him on [account of] his mighty acts: praise him according to his abundant greatness.
3 Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
Praise him with the sound of a trumpet: praise him with psaltery and harp.
4 Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
Praise him with timbrel and dance: praise him with stringed instruments and the organ.
5 Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
Praise him with melodious cymbals: praise him with loud cymbals.
6 Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.
Let every thing that has breath praise the Lord.