< Masalimo 15 >
1 Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
Psalm Dawida. PANIE, kto będzie przebywał w twoim przybytku? Kto zamieszka na twojej świętej górze?
2 Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
[Ten], kto postępuje nienagannie i czyni sprawiedliwość, a w swoim sercu mówi prawdę;
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
Kto nie obmawia swym językiem, nie wyrządza bliźniemu nic złego, nie znieważa bliźniego;
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
Ten, przed którego oczami bezbożny jest wzgardzony, a który szanuje [tych], co się boją PANA; kto, choć przysięga na własną niekorzyść, nie wycofuje się;
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.
Kto swych pieniędzy nie pożycza na lichwę i nie daje się przekupić przeciwko niewinnemu. Kto tak postępuje, nigdy się nie zachwieje.