< Masalimo 15 >

1 Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
Ihubo likaDavida. Thixo, ngubani ongahlala endlini yakho engcwele na? Ngubani ongahlala entabeni yakho engcwele na?
2 Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
Ngulowo okuhamba kwakhe kungelansolo njalo owenza okulungileyo, okhuluma iqiniso liphuma enhliziyweni yakhe,
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
ongachothoziyo ngolimi lwakhe, ongoneli umakhelwane wakhe futhi ongagconi umzalwane wakhe,
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
oweyisa umuntu oxhwalileyo kodwa ohlonipha labo abesaba uThixo, ogcina isifungo sakhe loba kubuhlungu ukwenzenjalo,
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.
owebolekisa imali yakhe engadingi inzuzo njalo owalayo ukuthengwa ukuze kwetheswe umlandu kongelacala. Lowo owenza lezizinto akayikuzanyazanyiswa lanini.

< Masalimo 15 >