< Masalimo 15 >

1 Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
Psaume de David. Éternel, qui séjournera dans ton tabernacle? Qui habitera sur ta montagne sainte?
2 Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
C'est celui qui marche dans l'intégrité, qui pratique la justice, Qui dit la vérité telle qu'elle est dans son coeur;
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
Celui dont la langue ne sème point la calomnie, Qui ne fait pas de mal à son semblable. Et qui ne jette pas l'opprobre sur son prochain.
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
Lui-même se sent indigne et méprisable; Mais il honore ceux qui craignent l'Éternel. S'il a juré, fût-ce à son préjudice, Il ne change rien à son serment.
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.
Il ne prête pas son argent à usure; Il n'accepte pas de présent contre l'innocent. Celui qui agit ainsi ne sera jamais ébranlé!

< Masalimo 15 >