< Masalimo 15 >
1 Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
Psaume de David. Eternel, qui est-ce qui séjournera dans ton Tabernacle? qui est-ce qui habitera en la montagne de ta Sainteté?
2 Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
Ce sera celui qui marche dans l'intégrité, qui fait ce qui est juste, et qui profère la vérité telle qu'elle est dans son cœur;
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
Qui ne médit point par sa langue, qui ne fait point de mal à son ami, qui ne diffame point son prochain;
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
Aux yeux duquel est méprisable celui qui mérite d'être rejeté, mais il honore ceux qui craignent l'Eternel; s'il a juré, fût-ce à son dommage, il n'en changera rien;
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.
Qui ne donne point son argent à usure, et qui ne prend point de présent contre l'innocent; celui qui fait ces choses, ne sera jamais ébranlé.