< Masalimo 15 >

1 Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
Davidin Psalmi. Herra, kuka asuu sinun majassas? eli kuka on pysyväinen sinun pyhällä vuorellas?
2 Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
Joka vaeltaa ja tekee oikeuden, ja puhuu totuuden sydämestänsä;
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
Joka ei kielellänsä panettele, eikä lähimmäisellensä mitään pahaa tee, ja ei häpäise lähimmäistänsä;
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
Joka jumalattomat katsoo ylön, vaan kunnioittaa Jumalaa pelkääväisiä; joka lähimmäisellensä vannoo ja pitää.
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.
Joka ei anna rahaansa korolle, eikä ota lahjoja viatointa vastaan. Joka näin tekee, ei hän horjahda ijankaikkisesti.

< Masalimo 15 >