< Masalimo 15 >
1 Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
A Psalm by David. LORD, who shall dwell in your sanctuary? Who shall live on your holy hill?
2 Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
He who walks blamelessly and does what is right, and speaks truth in his heart;
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
he who doesn’t slander with his tongue, nor does evil to his friend, nor casts slurs against his fellow man;
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
in whose eyes a vile man is despised, but who honors those who fear the LORD; he who keeps an oath even when it hurts, and doesn’t change;
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.
he who doesn’t lend out his money for usury, nor take a bribe against the innocent. He who does these things shall never be shaken.