< Masalimo 15 >
1 Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
“A psalm of David.” LORD, who shall abide at thy tabernacle? Who shall dwell upon thy holy hill?
2 Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
He that walketh uprightly, and doeth righteousness, And speaketh the truth from his heart;
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
He that slandereth not with his tongue, That doeth no injury to his neighbor, And uttereth no reproach against his neighbor;
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
In whose eyes a vile person is contemned; But who honoreth them that fear the LORD; Who sweareth to his own hurt, and changeth not;
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.
He that lendeth not his money for interest, And taketh not a bribe against the innocent: He that doeth these things shall never be moved.