< Masalimo 15 >

1 Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
[A Psalm by David.] YHWH, who shall dwell in your sanctuary? Who shall live on your holy mountain?
2 Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
He who walks blamelessly and does what is right, and speaks truth in his heart.
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
He doesn't slander with his tongue, nor does evil to his friend, nor lifts up an insult against his neighbor.
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
In his eyes a vile man is despised, but he honors those who fear YHWH. He keeps an oath even when it hurts, and doesn't change it.
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.
He doesn't lend out his money for interest, nor take a bribe against the innocent. The one who does these things will never be upended.

< Masalimo 15 >