< Masalimo 15 >
1 Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
A Psalm of David. O Lord, who shall sojourn in thy tabernacle? and who shall dwell in thy holy mountain?
2 Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
He that walks blameless, and works righteousness, who speaks truth in his heart.
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
Who has not spoken craftily with is tongue, neither has done evil to his neighbour, nor taken up a reproach against them that dwelt nearest to him.
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
In his sight an evil-worker is set at nought, but he honours them that fear the Lord. He swears to his neighbour, and disappoints [him] not.
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.
He has not lent his money on usury, and has not received bribes against the innocent. He that does these things shall never be moved.