< Masalimo 149 >

1 Tamandani Yehova. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, matamando ake mu msonkhano wa oyera mtima.
Msifuni Yahwe. Mwimbieni Yahwe wimbo mpya; imbeni sifa zake katika kusanyiko la waaminifu.
2 Israeli asangalale mwa mlengi wake; anthu a ku Ziyoni akondwere mwa Mfumu yawo.
Israeli ishangilie katika yeye aliye iumba; watu wa Sayuni na washangilie katika mfalme wao.
3 Atamande dzina lake povina ndi kuyimbira Iye nyimbo ndi tambolini ndi pangwe.
Nao walisifu jina lake kwa kucheza; na wamuimbie sifa yeye kwa ngoma na kinubi.
4 Pakuti Yehova amakondwera ndi anthu ake; Iye amaveka chipulumutso odzichepetsa.
Kwa kuwa Yahwe hupata furaha katika watu wake; huwapa utukufu wanyeyekevu kwa wokovu.
5 Oyera mtima asangalale mu ulemu wake ndi kuyimba mwachimwemwe pa mabedi awo.
Wacha Mungu wauchangilie ushindi; nao waimbe kwa furaha vitandani mwao.
6 Matamando a Mulungu akhale pakamwa pawo, ndi lupanga lakuthwa konsekonse mʼmanja mwawo,
Sifa za Mungu na ziwe vinywani mwao na panga mbili zenye makali mkononi mwao
7 kubwezera chilango anthu a mitundu ina, ndi kulanga anthu a mitundu yonse,
kutekeleza kisasi juu ya mataifa na matendo ya adhabu juu ya watu.
8 kumanga mafumu awo ndi zingwe, anthu awo otchuka ndi unyolo wachitsulo,
Nao watawafunga wafalme wao kwa minyororo na wakuu wao kwa pingu za chuma. Watatekeleza hukumu ambayo imeandikwa.
9 kuchita zimene zinalembedwa zotsutsana nawo Uwu ndi ulemerero wa oyera mtima ake onse. Tamandani Yehova.
Hii itakuwa ni heshima kwa ajili ya watakatifu wake wote. Msifuni Yahwe.

< Masalimo 149 >