< Masalimo 148 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani Yehova, inu a kumwamba, mutamandeni Iye, inu a mlengalenga.
Msifuni Bwana. Msifuni Bwana kutoka mbinguni, msifuni juu vileleni.
2 Mutamandeni, inu angelo ake onse, mutamandeni, mutamandeni, inu zolengedwa za mmwamba.
Msifuni, enyi malaika wake wote, msifuni yeye, enyi jeshi lake lote la mbinguni.
3 Mutamandeni, inu dzuwa ndi mwezi, mutamandeni, inu nonse nyenyezi zowala.
Msifuni yeye, enyi jua na mwezi, msifuni yeye, enyi nyota zote zingʼaazo.
4 Mutamandeni, inu thambo la kumwambamwamba ndi inu madzi a pamwamba pa thambo.
Msifuni yeye, enyi mbingu zilizo juu sana, na ninyi maji juu ya anga.
5 Zonse zitamande dzina la Yehova pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa.
Vilisifu jina la Bwana kwa maana aliamuru navyo vikaumbwa.
6 Iye anaziyika pa malo ake ku nthawi za nthawi; analamula ndipo sizidzatha.
Aliviweka mahali pake milele na milele, alitoa amri ambayo haibadiliki milele.
7 Tamandani Yehova pa dziko lapansi, inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya,
Mtukuzeni Bwana kutoka duniani, ninyi viumbe vikubwa vya baharini na vilindi vyote vya bahari,
8 inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo, mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake,
umeme wa radi na mvua ya mawe, theluji na mawingu, pepo za dhoruba zinazofanya amri zake,
9 inu mapiri ndi zitunda zonse, inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse,
ninyi milima na vilima vyote, miti ya matunda na mierezi yote,
10 inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse, inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka.
wanyama wa mwituni na mifugo yote, viumbe vidogo na ndege warukao,
11 Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse, inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi.
wafalme wa dunia na mataifa yote, ninyi wakuu na watawala wote wa dunia,
12 Inu anyamata ndi anamwali, inu nkhalamba ndi ana omwe.
wanaume vijana na wanawali, wazee na watoto.
13 Onsewo atamande dzina la Yehova pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka; ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe.
Wote na walisifu jina la Bwana, kwa maana jina lake pekee limetukuka, utukufu wake uko juu ya nchi na mbingu.
14 Iye wakwezera nyanga anthu ake, matamando a anthu ake onse oyera mtima, Aisraeli, anthu a pamtima pake. Tamandani Yehova.
Amewainulia watu wake pembe, sifa ya watakatifu wake wote, ya Israeli, watu walio karibu na moyo wake. Msifuni Bwana.

< Masalimo 148 >