< Masalimo 147 >
1 Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
Alaba al Señor; porque es bueno hacer melodía a nuestro Dios; la alabanza es agradable y hermosa.
2 Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
El Señor edifica a Jerusalén; hace que todos los desterrados de Israel se unan.
3 Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
Él hace que el corazón quebrantado sea bueno, y les echa aceite sobre sus heridas.
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
Él ve el número de las estrellas; él les da todos sus nombres.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
Grande es nuestro Señor, y grande su poder; no hay límite para su sabiduría.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
El Señor da ayuda a los pobres en espíritu; pero él envía a los pecadores avergonzados.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Haz canciones de alabanza al Señor; hacer melodía a nuestro Dios con instrumentos de música.
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
Por su mano el cielo está cubierto de nubes y la lluvia se almacena para la tierra; él hace que la hierba sea alta en las montañas.
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
Él da alimento a toda bestia, y a los cuervos jóvenes en respuesta a su clamor.
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
Él no tiene deleite en la fuerza de un caballo; él no disfruta de las piernas de un hombre.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
El Señor se complace en sus adoradores, y en aquellos cuya esperanza está en su misericordia.
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
Alaben al Señor, oh Jerusalén; alaben a su Dios, oh Sión.
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
Hizo fuertes las ataduras de hierro de tus puertas; él ha enviado bendiciones a tus hijos dentro de tus paredes.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
Él da paz en toda tu tierra, haciendo tus tiendas llenas de grano gordo.
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
Él envía sus órdenes a la tierra; su palabra sale rápidamente.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
Él da la nieve como la lana; él envía gotas de hielo como el polvo.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
Hace caer el hielo como gotas de lluvia: el agua se endurece por el frío.
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
Al pronunciar su palabra, el hielo se convierte en agua; cuando él envía su viento, hay un flujo de aguas.
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
Él le aclara su palabra a Jacob, enseñando a Israel sus leyes y sus decisiones.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.
No hizo estas cosas por ninguna otra nación; y en cuanto a sus leyes, no las conocen. Dejen que el Señor sea alabado.