< Masalimo 147 >

1 Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
Alabád a Jehová; porque es bueno cantar salmos a nuestro Dios; porque suave y hermosa es la alabanza.
2 Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
El que edifica a Jerusalem, Jehová: los echados de Israel recogerá.
3 Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
El que sana a los quebrantados de corazón; y el que liga sus dolores.
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
El que cuenta el número de las estrellas, y a todas ellas llama por sus nombres.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
Grande es el Señor nuestro, y de mucho poder; y de su entendimiento no hay número.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
El que ensalza a los humildes, Jehová: el que humilla a los impíos hasta la tierra.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Cantád a Jehová con alabanza: cantád a nuestro Dios con arpa.
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
El que cubre los cielos de nubes; el que apareja la lluvia para la tierra: el que hace a los montes producir yerba.
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
El que da a la bestia su mantenimiento: a los hijos de los cuervos que claman a él.
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
No toma contentamiento en la fortaleza del caballo: ni se deleita con las piernas del varón.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
Ama Jehová a los que le temen: a los que esperan en su misericordia.
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
Alaba, Jerusalem, a Jehová: alaba, Sión, a tu Dios.
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
Porque fortificó los cerrojos de tus puertas: bendijo a tus hijos dentro de ti.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
El que pone por tu término la paz; y de grosura de trigo te hará hartar.
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
El que envía su palabra a la tierra; y muy presto corre su palabra.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
El que da la nieve como lana: derrama la helada como ceniza.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
El que echa su hielo como en pedazos; ¿delante de su frío quién estará?
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
Enviará su palabra, y desleirlos ha: soplará su viento, gotearán las aguas.
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
El que denuncia sus palabras a Jacob, sus estatutos y sus juicios a Israel.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.
No ha hecho esto con toda nación; y sus juicios no los conocieron. Alelu- Jah.

< Masalimo 147 >