< Masalimo 147 >

1 Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
Dumisani iNkosi, ngoba kuhle ukuhlabelela indumiso kuNkulunkulu wethu, ngoba kumnandi, indumiso ifanele.
2 Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
INkosi iyayakha iJerusalema, iqoqe abahlakaziweyo bakoIsrayeli.
3 Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
Yelapha abadabukileyo enhliziyweni, ibophe izinsizi zabo.
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
Ibala inani lezinkanyezi, izibize zonke ngamabizo.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
Yinkulu iNkosi yethu, njalo ngeyamandla amakhulu; ukuqedisisa kwayo kakulakunaniswa.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
INkosi iyaphakamisa abamnene, iyabawisela emhlabathini ababi.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Hlabelelani eNkosini ngokubonga; lihlabele indumiso kuNkulunkulu wethu ngechacho.
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
Eyembesa amazulu ngamayezi, elungisela umhlaba izulu, ekhulisa utshani ezintabeni,
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
enika inyamazana ukudla kwazo, amaphuphu ewabayi akhalayo.
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
Kayithokozi ngamandla ebhiza, kayijabuleli imilenze yomuntu.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
INkosi ijabulela abayesabayo, labo abathembela emuseni wayo.
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
Babaza iNkosi, Jerusalema. Dumisa uNkulunkulu wakho, Ziyoni.
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
Ngoba iqinise imigoqo yamasango akho; ibusise abantwana bakho phakathi kwakho.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
Iyenza ukuthula emingceleni yakho; ikusuthise ngamanono engqoloyi.
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
Iyathumela umthetho wayo emhlabeni; ilizwi layo ligijima ngesiqubu esikhulu.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
Enika iliqhwa elikhithikileyo njengoboya bezimvu; ihaze ungqwaqwane njengomlotha.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
Iyaphosa isiqhotho sayo njengezigaqa; ngubani ongema phambi komqando wayo?
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
Iyathumela ilizwi layo, ikuncibilikise; ivunguzise umoya wayo, amanzi ageleze.
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
Iyamemezela ilizwi layo kuJakobe, izimiso zayo lezahlulelo zayo kuIsrayeli.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.
Kayenzanga njalo lakusiphi isizwe; lezahlulelo zayo kazizazi. Dumisani iNkosi!

< Masalimo 147 >