< Masalimo 147 >
1 Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
Yabi Ubangiji. Yana da kyau a rera yabai ga Allahnmu, abu mai daɗi ne daidai ne kuma a yabe shi!
2 Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
Ubangiji ya gina Urushalima; ya tattara kamammu na Isra’ilan da aka kai bauta.
3 Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
Ya warkar da masu raunanar zuciya ya ɗaɗɗaura miyakunsu.
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
Ya lissafta yawan taurari ya kuma kira kowannensu da suna.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
Shugabanmu mai girma ne mai iko duka; ganewarsa ba shi da iyaka.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
Ubangiji yana kula da masu sauƙinkai yakan yar da mugaye a ƙasa.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Rera wa Ubangiji waƙar godiya; ku kada garaya ga Allahnmu.
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
Ya rufe sararin sama da gizagizai; yana tanada wa duniya ruwan sama yana kuma sa ciyawa tă yi girma a kan tuddai.
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
Yakan tanada wa shanu abinci da kuma saboda’ya’yan hankaki sa’ad da suka yi kira.
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
Jin daɗinsa ba ya a ƙarfin doki, balle farin cikinsa yă kasance a ƙafafun mutum;
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
Ubangiji yakan yi farin ciki a waɗanda suke tsoronsa, waɗanda suke sa zuciya a ƙaunarsa marar ƙarewa.
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
Ki ɗaukaka Ubangiji, ya Urushalima; ki yabi Allahnki, ya Sihiyona.
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
Gama yana ƙarfafa ƙyamaren ƙofofinki yana kuma albarkace mutanenki a cikinki.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
Yana ba da salama ga iyakokinki yana kuma ƙosar da ke da alkama mafi kyau.
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
Yana ba da umarninsa ga duniya; maganarsa tana tafiya da sauri.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
Yana shimfiɗa ƙanƙara kamar ulu yă kuma watsar da hazo kamar toka.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
Yana zuba ƙanƙara kamar ƙananan duwatsu. Wa zai iya jure wa sanyin da ya aiko?
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
Yakan aiki maganarsa ta kuwa narkar da su; yakan tā da iskarsa, ruwaye kuwa su gudu.
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
Ya bayyana maganarsa ga Yaƙub, dokokinsa da ƙa’idodinsa ga Isra’ila.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.
Bai yi wannan ga wata al’umma ba; ba su san dokokinsa ba. Yabi Ubangiji.