< Masalimo 147 >
1 Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
Preiset den HERRN! Denn schön ist’s, unserm Gott zu lobsingen, ja lieblich und wohlgeziemend ist Lobgesang.
2 Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
Der HERR baut Jerusalem wieder auf, er sammelt Israels zerstreute Söhne;
3 Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
er heilt, die zerbrochnen Herzens sind, und verbindet ihre Wunden;
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
er bestimmt den Sternen ihre Zahl und ruft sie alle mit Namen.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
Groß ist unser Herr und allgewaltig, für seine Weisheit gibt’s kein Maß.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
Der HERR hilft den Gebeugten auf, doch die Gottlosen stürzt er nieder zu Boden.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Stimmt für den HERRN ein Danklied an, spielt unserm Gott auf der Zither –
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
ihm, der den Himmel mit Wolken bedeckt und Regen schafft für die Erde, der Gras auf den Bergen sprießen läßt,
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
der den Tieren ihr Futter gibt, den jungen Raben, die zu ihm schreien!
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
Er hat nicht Lust an der Stärke des Rosses, nicht Gefallen an den Schenkeln des Mannes;
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
Gefallen hat der HERR an denen, die ihn fürchten, an denen, die auf seine Gnade harren.
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
Preise den HERRN, Jerusalem, lobsinge, Zion, deinem Gott!
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
Denn er hat die Riegel deiner Tore stark gemacht, gesegnet deine Kinder in deiner Mitte;
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
er schafft deinen Grenzen Sicherheit, sättigt dich mit dem Mark des Weizens.
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
Er läßt sein Machtwort nieder zur Erde gehn: gar eilig läuft sein Gebot dahin;
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
er sendet Schnee wie Wollflocken und streut den Reif wie Asche aus;
17 Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
er wirft seinen Hagel wie Brocken herab: wer kann bestehn vor seiner Kälte?
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
Doch läßt er sein Gebot ergehn, so macht er sie schmelzen; läßt er wehn seinen Tauwind, so rieseln die Wasser.
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
Er hat Jakob sein Wort verkündet, Israel sein Gesetz und seine Rechte.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.
Mit keinem (anderen) Volk ist so er verfahren, drum kennen sie seine Rechte nicht. Halleluja!