< Masalimo 147 >
1 Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
Alléluia.
2 Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
Bâtissant Jérusalem, le Seigneur rassemblera les dispersions d’Israël.
3 Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
C’est lui qui guérit ceux qui ont le cœur brisé, et qui bande leurs plaies.
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
Qui compte la multitude des étoiles, et à elles toutes donne des noms.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
Grand est notre Dieu, et grande est sa force; et à sa sagesse il n’y a point de borne.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
Le Seigneur prend sous sa protection les hommes doux; mais il humilie les pécheurs jusqu’à terre.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Entonnez au Seigneur une louange: chantez notre Dieu sur la harpe.
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
C’est lui qui couvre le ciel de nuages, et prépare à la terre de la pluie. Qui produit sur les montagnes du foin, et de l’herbe à l’usage des hommes.
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
Qui donne aux bêtes leur nourriture, et aux petits des corbeaux qui l’invoquent.
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
Ce n’est pas dans la force du cheval qu’il mettra son désir, ni dans les jambes de l’homme qu’il se complaira.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
Le Seigneur a mis sa complaisance dans ceux qui le craignent, et dans ceux qui espèrent en sa miséricorde.
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
Jérusalem, loue le Seigneur: loue ton Dieu, ô Sion.
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
Parce qu’il a affermi les serrures de tes portes: il a béni tes fils au milieu de toi.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
C’est lui qui a établi sur tes confins la paix, et qui te rassasie de moelle de froment.
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
C’est lui qui envoie sa parole à la terre: avec vitesse court sa parole.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
C’est lui qui donne de la neige comme de la laine, répand le brouillard comme de la cendre.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
Il envoie sa glace comme des petits morceaux de pain: à la face de son froid qui tiendra?
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
Il enverra sa parole, et il les fera fondre: son vent soufflera, et les eaux couleront.
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
C’est lui qui annonce sa parole à Jacob; ses justices et ses jugements à Israël.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.
Il n’a pas fait ainsi pour toute nation: et ses jugements, il ne les leur a pas manifestés. Alléluia.