< Masalimo 147 >

1 Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
Praise JAH, for it is good to sing praises to our God; for it is pleasant and fitting to praise him.
2 Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
YHWH builds up Jerusalem. He gathers together the outcasts of Israel.
3 Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
He heals the broken in heart, and binds up their wounds.
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
He counts the number of the stars. He calls them all by their names.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
Great is our Lord, and mighty in power. His understanding is infinite.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
YHWH upholds the humble. He brings the wicked down to the ground.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Sing to YHWH with thanksgiving. Sing praises on the harp to our God,
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
who covers the sky with clouds, who prepares rain for the earth, who makes grass grow on the mountains.
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
He provides food for the livestock, and for the young ravens when they call.
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
He doesn't delight in the strength of the horse. He takes no pleasure in the legs of a man.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
YHWH takes pleasure in those who fear him, in those who hope in his loving kindness.
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
Praise YHWH, Jerusalem. Praise your God, Zion.
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
For he has strengthened the bars of your gates. He has blessed your children within you.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
He makes peace in your borders. He fills you with the finest of the wheat.
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
He sends out his commandment to the earth. His word runs very swiftly.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
He gives snow like wool, and scatters frost like ashes.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
He hurls down his hail like pebbles. Who can stand before his cold?
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
He sends out his word, and melts them. He causes his wind to blow, and the waters flow.
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
He shows his word to Jacob; his statutes and his ordinances to Israel.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.
He has not done this for just any nation. They do not know his ordinances. Praise JAH.

< Masalimo 147 >