< Masalimo 147 >
1 Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
Aleluja! Hvalite Jahvu jer je dobar, pjevajte Bogu našem jer je sladak; svake hvale on je dostojan!
2 Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
Jahve gradi Jeruzalem, sabire raspršene Izraelce.
3 Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
On liječi one koji su srca skršena i povija rane njihove.
4 Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
On određuje broj zvijezda, svaku njezinim imenom naziva.
5 Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
Velik je naš Gospodin i svesilan, nema mjere mudrosti njegovoj.
6 Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
Jahve pridiže ponizne, zlotvore do zemlje snizuje.
7 Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
Pjevajte Jahvi pjesmu zahvalnu, svirajte na citari Bogu našem!
8 Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
Oblacima on prekriva nebesa i zemlji kišu sprema; daje da po bregovima raste trava i bilje na službu čovjeku.
9 Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
On stoci hranu daje i mladim gavranima kada grakću.
10 Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
Za konjsku snagu on ne mari nit' mu se mile bedra čovječja.
11 Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
Mili su Jahvi oni koji se njega boje, koji se uzdaju u dobrotu njegovu.
12 Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
Slavi Jahvu, Jeruzaleme, hvali Boga svoga, Sione!
13 pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
On učvrsti zasune vrata tvojih, blagoslovi u tebi tvoje sinove.
14 Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
On dade mir granicama tvojim, pšenicom te hrani najboljom.
15 Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
Besjedu svoju šalje na zemlju, brzo trči riječ njegova.
16 Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
Kao vunu snijeg razbacuje, prosipa mraz poput pepela.
17 Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
On sipa grÓad kao zalogaje, voda mrzne od njegove studeni.
18 Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
Riječ svoju pošalje i vode se tope; dunu vjetrom i vode otječu.
19 Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
Riječ svoju on objavi Jakovu, odluke svoje i zakone Izraelu.
20 Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.
Ne učini tako nijednom narodu: nijednom naredbe svoje ne objavi! Aleluja!