< Masalimo 146 >
1 Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Louez l'Éternel! Mon âme, loue l'Éternel!
2 Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
Je louerai l'Éternel tant que je vivrai; je célébrerai mon Dieu tant que j'existerai.
3 Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
Ne vous confiez pas dans les grands, ni dans aucun fils d'homme, qui ne saurait délivrer.
4 Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
Son souffle s'en va, il retourne à sa terre, et en ce jour-là ses desseins périssent.
5 Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
Heureux celui qui a le Dieu de Jacob pour aide, et dont l'attente est en l'Éternel son Dieu,
6 Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
Qui a fait les cieux et la terre, la mer et tout ce qui y est; qui garde la fidélité à toujours;
7 Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
Qui fait droit à ceux qui sont opprimés, qui donne du pain à ceux qui ont faim!
8 Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
L'Éternel délie les captifs; l'Éternel ouvre les yeux des aveugles; l'Éternel redresse ceux qui sont courbés; l'Éternel aime les justes.
9 Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
L'Éternel garde les étrangers; il soutient l'orphelin et la veuve; mais il renverse la voie des méchants.
10 Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.
L'Éternel régnera éternellement. O Sion, ton Dieu est d'âge en âge! Louez l'Éternel!