< Masalimo 146 >

1 Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Praise ye the LORD. Praise the LORD, O my soul.
2 Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
While I live will I praise the LORD: I will sing praises unto my God while I have any being.
3 Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
Put not your trust in princes, [nor] in the son of man, in whom [there is] no help.
4 Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
His breath goeth forth, he returneth to his earth; in that very day his thoughts perish.
5 Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
Happy [is he] that [hath] the God of Jacob for his help, whose hope [is] in the LORD his God:
6 Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
Which made heaven, and earth, the sea, and all that therein [is: ] which keepeth truth for ever:
7 Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
Which executeth judgment for the oppressed: which giveth food to the hungry. The LORD looseth the prisoners:
8 Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
The LORD openeth [the eyes of] the blind: the LORD raiseth them that are bowed down: the LORD loveth the righteous:
9 Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
The LORD preserveth the strangers; he relieveth the fatherless and widow: but the way of the wicked he turneth upside down.
10 Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.
The LORD shall reign for ever, [even] thy God, O Zion, unto all generations. Praise ye the LORD.

< Masalimo 146 >