< Masalimo 146 >

1 Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Alleluia, [a Psalm] of Aggaeus and Zacharias. My soul, praise the Lord.
2 Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
While I live will I praise the Lord: I will sing praises to my God as long as I exist.
3 Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
Trust not in princes, nor in the children of men, in whom there is no safety.
4 Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
His breath shall go forth, and he shall return to his earth; in that day all his thoughts shall perish.
5 Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
Blessed is he whose helper is the God of Jacob, whose hope is in the Lord his God:
6 Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
who made heaven, and earth, the sea, and all things in them: who keeps truth for ever:
7 Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
who executes judgment for the wronged: who gives food to the hungry. The Lord looses the fettered ones:
8 Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
the Lord gives wisdom to the blind: The Lord sets up the broken down: the Lord loves the righteous: the Lord preserves the strangers;
9 Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
he will relieve the orphan and widow: but will utterly remove the way of sinners.
10 Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.
The Lord shall reign for ever, [even] thy God, O Sion, to all generations.

< Masalimo 146 >