< Masalimo 145 >

1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Хвала́ Давидова.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Я кожного дня Тебе благословля́тиму, і хвалитиму Йме́ння Твоє повік-віку!
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Великий Господь і просла́влений ве́льми, і недосліди́ме вели́ччя Його!
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Рід ро́дові буде хвалити діла́ Івої, і будуть могу́тність Твою виявляти!
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Про пишну славу вели́ччя Твого, про справи чудо́вні Твої розпові́м!
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Будуть казати про силу грізни́х Твоїх чи́нів, а про ве́лич Твою — розпові́м я про неї.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Па́м'ять про добрість велику Твою сповіща́тимуть, і будуть співати про правду Твою!
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Ще́дрий і милосердний Господь, довготерпели́вий й многомилости́вий,
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
Господь добрий до всіх, а Його милосердя — на всі Його тво́рива!
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Тебе, Господи, сла́вити будуть усі Твої тво́рива, а святі Твої Тебе благословля́тимуть,
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
про славу Царства Твого звіща́тимуть, про могутність Твою говори́тимуть,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
щоб лю́дським синам об'яви́ти про могутність Його́ та про славу вели́ччя Царства Його́!
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Царство Твоє — царство всіх віків, а вла́да Твоя — по всі роди!
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
Господь підпира́є всіх па́даючих, усіх зі́гнутих Він випросто́вує!
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Очі всіх упова́ють на Те́бе, і Ти їм пожи́ву даєш своєча́сно,
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Ти руку Свою відкрива́єш, — і все, що живе, Ти зичли́во году́єш!
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Господь справедливий на кожній дорозі Своїй, і милости́вий у всіх Своїх учи́нках,
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Господь близьки́й всім, хто взива́є до Нього, хто правдою кличе Його́!
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Волю тих, хто боїться Його, Він сповня́є, і блага́ння їх чує та їм помагає, —
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
Госпо́дь береже́ тих усіх, хто любить Його, а безбожних усіх Він понищить!
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Славу Господню уста́ мої будуть звіща́ти, і благословля́тиме кожне тіло святе Його Ймення на віки вікі́в!

< Masalimo 145 >