< Masalimo 145 >
1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Nitakutukuza wewe, Mungu wangu, Mfalme; nitalihimidi jina lako milele na milele.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Kila siku nitakuhimidi; nitalisifu jina lako milele na milele.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Yahwe ndiye mkuu na wakusifiwa sana; ukuu wake hauchunguziki.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Kizazi kimoja kitayasifu matendo yako kwa kizazi kijacho na kitatangaza matendo yako makuu.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Nitaitafakari fahari ya utukufu wa adhama yako na matendo yako ajabu.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Watanena juu ya nguvu ya kazi zako za kutisha, nami nitatangaza ukuu wako.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Nao watatangaza wingi wa wema wako, na wataimba kuhusu haki yako.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Yahwe ni wa neema na huruma, si mwepesi wa hasira na mwingi katika uaminifu wa agano lake.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
Yahwe ni mwema kwa wote; huruma zake zi juu ya kazi zake zote.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Vyote ulivyo viumba vitakushukuru wewe, Yahwe; waaminifu wako watakutukuza wewe.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
Waaminifu wako watanena juu ya utukufu wa ufalme wako, na watahubiri juu ya nguvu zako.
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
Watayafanya matendo makuu ya Mungu ya julikane na wanadamu na utukufu wa fahari ya ufalme wake.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Ufalme wako ni wa milele, na mamlaka yako ya dumu kizazi hata kizazi.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
Yahwe huwategemeza wote waangukao na huwainua wote walioinama chini.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Macho ya wote yanakungoja wewe; nawe huwapa chakula chao kwa wakati sahihi.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Huufungua mkono wako na hukidhi haja ya kila kiumbe hai.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Yahwe ni mwenye haki katika njia zake zote na neema katika yote afanyayo.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Yahwe yu karibu na wote wamwitao, wale wamwitao yeye katika uaminifu.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Hutimiza haja za wale wanao mheshimu yeye; husikia kilio chao na kuwaokoa.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
Yahwe huwalinda wale wampendao, lakini atawaangamiza waovu wote.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Kinywa changu kitazinena sifa za Yahwe; wanadamu wote na walitukuze jina lake takatifu milele na milele.