< Masalimo 145 >

1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Hvala Davidova. Poviševal te bodem, Bog moj, kralj; in blagoslavljal bodem ime tvoje vekomaj in vekomaj.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Vsak dan te bodem blagoslavljal, in hvalil ime tvoje vekomaj in vekomaj.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Velik je Gospod in hvale vreden jako; dà, velikosti njegove ni preiskati.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Rod naj rodú slavi dela tvoja; kakor ona oznanjajo vsakotero mogočnost tvojo.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Lepoto in slavo tvojega veličastva, in čudovite stvari tvoje bodem oznanjal.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
In moč čudovitih dél tvojih naj slavé; in posamezna velika dela tvoja bodem pripovedoval.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Spomin obile dobrote tvoje naj vrè iz njih; pravico tvojo naj pojó.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Milosten in usmiljen je Gospod; potrpežljiv in velik v milosti.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
Dober je Gospod vsem; in usmiljenje njegovo v vseh delih njegovih.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Slavé te naj, Gospod, vsa dela tvoja; in blagoslavljajo te naj, katerim milost izkazuješ.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
Slavo kraljestva tvojega naj slavé, in naznanjajo mogočnost tvojo.
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
Da sinom človeškim oznanjajo mogočnost njegovo, in slavo in lepoto njegovega kraljestva.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Kraljestvo tvoje je vseh vekov kraljestvo, in gospostvo tvoje od roda do roda.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
Gospod podpira vse padajoče, in kvišku pomaga vsem omahujočim.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Vseh oči gledajo v té; ti jim daješ jedi o svojem času.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Roko svojo odpreš in nasitiš karkoli živi, po volji.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Pravičen je Gospod po vseh potih svojih, in dobrotljiv v vseh svojih delih.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Blizu je Gospod vsem, ki ga kličejo; vsem, kateri ga kličejo v zvestobi.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Voljo spolnjuje boječim se njega; vpitje njih sliši in daje jim blaginjo.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
Gospod hrani vse, kateri ga ljubijo; vse hudobne pa pogublja.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Hvalo Gospodovo naj govoré usta moja; in vse meso naj blagoslavlja sveto ime njegovo, vekomaj in vekomaj.

< Masalimo 145 >