< Masalimo 145 >

1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
I PAN kapinga komui, ai Kot o Nanmarki, o kapinga mar omui ansau karos kokolata.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
I pan kapinga komui ni ran akan karos, o kapinga mar omui ansau kan karos kokolata.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Ieowa meid lapalap, o kapingapan, o sota me kak dedeki duen a lapalap.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Seri en seri kan pan kapinga omui dodok kan, o kasokasoi duen omui manaman.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
I pan kasokasoia duen lingan en omui kapwat, o i pan kauleki duen omui manaman akan.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
O re pan kasokasoia duen manaman en omui dodok kan, o pan kapakaparok duen omui lapalap.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Irail pan kasokasoia duen omui kalangan lapalap, o pereperen o kapinga duen omui pung.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Ieowa me dir en mak o kapunglol, kanongama o limpok.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
Ieowa me kalangan ong karos o a kapunglol ong a wiawia kan karos.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Sapwilim omui wiawia kan en kapinga komui. Maing Ieowa, o sapwilim omui lelapok kan en kapinga komui.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
O ren kasokasoia duen lingan en wei omui, o ren kapakaparokki duen omui manaman.
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
Pwe aramas akan en dedeki duen omui manaman o lingan ong wei omui.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Wei omui wei soutuk eu, o omui kakaun pan duedueta kokolata.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
Ieowa kin kotin kolekol karos, me pan pupedi, o kainsen maula karos, me mamauk.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Por en mas karos kasikasik komui, o kom kotiki ong ir kan ar kisin manga ni ar ansau.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Kom kotiki pasang lim omui o kadirela karos, me memaur, duen kupur omui.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Ieowa me pung ni al a karos o saraui ni a wiawia kan karos.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Ieowa kotikot ren karos, me likwir ong i, karos, me likwir melel.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
A kotin wiai ong, me masak i duen ar inong. A kotin mangi ar ngidingid, ap kotin sauasa ir.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
Ieowa kin kotin sinsila karos, me pok ong i, a pan kamela me doo sang Kot akan karos.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Au ai pan kapinga Ieowa, o uduk karos kapinga mar a saraui ansau kan karos kokolata.

< Masalimo 145 >