< Masalimo 145 >

1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Ein lovsong av David. Eg vil upphøgja deg, min Gud, du konge, og eg vil lova namnet ditt æveleg og alltid.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Kvar dag vil eg lova deg, og eg vil prisa namnet ditt æveleg og alltid.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Stor er Herren og mykje lovsungen, og hans storleik er uransakleg.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Ei ætt skal lova dine verk for ei onnor, og dine storverk skal dei forkynna.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Di høge og herlege æra og dine underverk vil eg grunda på.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Um dine sterke, skræmelege gjerningar skal dei tala, og dine storverk vil eg fortelja um.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Minne-ord um din store godleik skal dei lata strøyma ut, og di rettferd skal dei lovsyngja.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Nådig og miskunnsam er Herren, langmodig og stor i miskunn.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
Herren er god imot alle, og han miskunnar alle sine verk.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Alle dine verk skal prisa deg, Herre, og dine trugne lova deg.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
Um herlegdomen i ditt rike skal dei tala, og ditt velde skal dei forkynna,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
til å kunngjera dine velduge verk for menneskjeborni, og den strålande herlegdom i ditt rike.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Ditt rike er eit rike for alle ævor, og ditt herredøme varer gjenom alle ætter.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
Herren er stydjar alle som fell, og han reiser alle som er nedbøygde.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Alle vender augo sine ventande til deg, og du gjev deim deira føda i si tid.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Du let upp handi og mettar alt levande med hugnad.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Herren er rettferdig på alle sine vegar og miskunnsam i alle sine verk.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Herren er nær hjå alle deim som kallar på honom, alle som kallar på honom i sanning.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Han gjer etter deira ynskje som ottast honom, og han høyrer deira rop og frelser deim.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
Herren varar alle deim som elskar honom, men alle ugudlege tyner han.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Min munn skal mæla um Herrens pris, og alt kjøt skal lova hans heilage namn i all æva og alltid.

< Masalimo 145 >