< Masalimo 145 >
1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
わがかみ王よわれ汝をあがめ 世かぎりなく聖名をほめまつらん
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
われ日ごとに汝をほめ世々かぎりなく聖名をはめたたへん
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
ヱホバは大にましませば最もほむべきかな その大なることは尋ねしることかたし
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
この代はかの代にむかひてなんぢの事跡をほめたたへ なんぢの大能のはたらきを宣つたへん
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
われ汝のほまれの榮光ある稜威となんぢの奇しきみわざとを深くおもはん
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
人はなんぢのおそるべき動作のいきほひをかたり 我はなんぢの大なることを宣つたへん
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
かれらはなんぢの大なる惠の跡をいひいで なんぢの義をほめうたはん
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
ヱホバは惠ふかく憐憫みち また怒りたまふことおそく憐憫おほいなり
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
ヱホバはよろづの者にめぐみあり そのふかき憐憫はみわざの上にあまねし
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
ヱホバよ汝のすべての事跡はなんぢに感謝し なんぢの聖徒はなんぢをほめん
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
かれらは御國のえいくわうをかたり汝のみちからを宣つたへて
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
その大能のはたらきとそのみくにの榮光あるみいづとを人の子輩にしらすべし
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
なんぢの國はとこしへの國なり なんぢの政治はよろづ代にたゆることなし
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
ヱホバはすべて倒れんとする者をささへ かがむものを直くたたしめたまふ
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
よろづのものの目はなんぢを待 なんぢは時にしたがひてかれらに糧をあたへ給ふ
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
なんぢ手をひらきてもろもろの生るものの願望をあかしめたまふ
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
ヱホバはそのすべての途にただしく そのすべての作爲にめぐみふかし
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
すべてヱホバをよぶもの 誠をもて之をよぶものに ヱホバは近くましますなり
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
ヱホバは己をおそるるものの願望をみちたらしめ その號呼をききて之をすくひたまふ
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
ヱホバはおのれを愛しむものをすべて守りたまへど 惡者をことごとく滅したまはん
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
わが口はヱホバの頌美をかたり よろづの民は世々かぎりなくそのきよき名をほめまつるべし