< Masalimo 145 >
1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
[Salmo di] lode, di Davide O DIO mio, Re mio, io ti esalterò; E benedirò il tuo Nome in sempiterno.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Io ti benedirò tuttodì; E loderò il tuo Nome in sempiterno.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Il Signore [è] grande, e degno di somma lode; E la sua grandezza non può essere investigata.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Un'età dopo l'altra predicherà le lodi delle tue opere; E gli uomini racconteranno le tue prodezze.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Io ragionerò della magnificenza della gloria della tua maestà, E delle tue maraviglie.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
E [gli uomini] diranno la potenza delle tue [opere] tremende; Ed io narrerò la tua grandezza.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Essi sgorgheranno la ricordanza della tua gran bontà, E canteranno con giubilo la tua giustizia.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Il Signore [è] grazioso, e pietoso; Lento all'ira, e di gran benignità.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
Il Signore [è] buono inverso tutti; E le sue compassioni [son] sopra tutte le sue opere.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
O Signore, tutte le tue opere ti celebreranno; E i tuoi santi ti benediranno:
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
Diranno la gloria del tuo regno; E narreranno la tua forza;
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
Per far note le tue prodezze, E la magnificenza della gloria del tuo regno a' figliuoli degli uomini.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Il tuo regno [è] un regno di tutti i secoli, E la tua signoria [è] per ogni età.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
Il Signore sostiene tutti quelli che cadono, E rileva tutti quelli che dichinano.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Gli occhi di tutti sperano in te; E tu dài loro il lor cibo al suo tempo.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Tu apri la tua mano, E sazii di benevolenza ogni vivente
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Il Signore [è] giusto in tutte le sue vie, E benigno in tutte le sue opere.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Il Signore [è] presso di tutti quelli che l'invocano, Di tutti quelli che l'invocano in verità.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Egli adempie il desiderio di quelli che lo temono, E ode il lor grido, e li salva.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
Il Signore guarda tutti quelli che l'amano; E distruggerà tutti gli empi.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
La mia bocca narrerà la lode del Signore; E ogni carne benedirà il Nome della sua santità In sempiterno.