< Masalimo 145 >

1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
O Dio, mio re, voglio esaltarti e benedire il tuo nome in eterno e per sempre. Lodi. Di Davide.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Ti voglio benedire ogni giorno, lodare il tuo nome in eterno e per sempre.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Grande è il Signore e degno di ogni lode, la sua grandezza non si può misurare.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Una generazione narra all'altra le tue opere, annunzia le tue meraviglie.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Proclamano lo splendore della tua gloria e raccontano i tuoi prodigi.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Dicono la stupenda tua potenza e parlano della tua grandezza.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Diffondono il ricordo della tua bontà immensa, acclamano la tua giustizia.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Paziente e misericordioso è il Signore, lento all'ira e ricco di grazia.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
Buono è il Signore verso tutti, la sua tenerezza si espande su tutte le creature.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Ti lodino, Signore, tutte le tue opere e ti benedicano i tuoi fedeli.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
Dicano la gloria del tuo regno e parlino della tua potenza,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
per manifestare agli uomini i tuoi prodigi e la splendida gloria del tuo regno.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Il tuo regno è regno di tutti i secoli, il tuo dominio si estende ad ogni generazione.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
Il Signore sostiene quelli che vacillano e rialza chiunque è caduto.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Gli occhi di tutti sono rivolti a te in attesa e tu provvedi loro il cibo a suo tempo.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Tu apri la tua mano e sazi la fame di ogni vivente.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Giusto è il Signore in tutte le sue vie, santo in tutte le sue opere.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Il Signore è vicino a quanti lo invocano, a quanti lo cercano con cuore sincero.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Appaga il desiderio di quelli che lo temono, ascolta il loro grido e li salva.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
Il Signore protegge quanti lo amano, ma disperde tutti gli empi.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Canti la mia bocca la lode del Signore e ogni vivente benedica il suo nome santo, in eterno e sempre.

< Masalimo 145 >