< Masalimo 145 >

1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Ein Loblied von David. Ich will dich erheben, mein Gott, du König,
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
An jedem Tage will ich dich preisen und deinen Namen rühmen immer und ewig!
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Groß ist der HERR und hoch zu rühmen, und seine Größe ist unausforschlich.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Ein Geschlecht wird dem andern rühmen deine Werke und kundtun deine gewaltigen Taten.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Von der herrlichen Pracht deiner Hoheit will ich reden, und von deinen Wundertaten (will ich singen).
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Von der Macht deines furchtbaren Waltens wird man reden, und deine Größe – davon will ich erzählen!
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Den Ruhm deiner reichen Güte wird man verkünden und jubelnd preisen deine Gerechtigkeit.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Gnädig und barmherzig ist der HERR, langmütig und reich an Güte.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
Der HERR ist gütig gegen alle, und sein Erbarmen umfaßt alle seine Werke.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Alle deine Werke werden dich loben, HERR, und deine Frommen dich preisen;
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
die Herrlichkeit deines Königtums werden sie rühmen und reden von deiner Macht,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
um den Menschenkindern kundzutun seine mächtigen Taten und die herrliche Pracht seines Königtums.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Dein Reich ist ein Reich für alle Ewigkeiten, und deine Herrschaft besteht durch alle Geschlechter. Getreu ist der HERR in seinen Worten und heilig in all seinem Tun.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
Der HERR stützt alle Fallenden und richtet alle Gebeugten auf.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Aller Augen warten auf dich, und du gibst ihnen ihre Speise zu seiner Zeit;
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
du tust deine Hand auf und sättigst alles, was lebt, mit Wohlgefallen.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Gerecht ist der HERR in all seinem Walten und liebreich in all seinem Tun.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Der HERR ist nahe allen, die ihn anrufen, allen, die ihn in Treue anrufen;
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
er erfüllt das Begehren derer, die ihn fürchten, er hört ihr Schreien und hilft ihnen.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
Der HERR behütet alle, die ihn lieben, doch alle Frevler rottet er aus.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Mein Mund soll verkünden den Lobpreis des HERRN, und alles Fleisch soll preisen seinen heiligen Namen immer und ewig!

< Masalimo 145 >