< Masalimo 145 >
1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Cantique de louanges. De David. Je l'exalterai, ô mon Dieu, ô mon Roi! et je bénirai ton nom toujours, à jamais.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Chaque jour je te bénirai, et je louerai ton nom éternellement, à jamais.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
L'Éternel est grand et très glorieux, et sa grandeur est incommensurable.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Qu'un âge à l'autre âge annonce tes œuvres, et publie tes exploits!
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
C'est la glorieuse majesté de ta magnificence, ce sont tes merveilles que je veux méditer.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Qu'on redise la puissance de tes exploits terribles, et je veux raconter ta grandeur!
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Que l'on proclame la mémoire de ta grande bonté, et que l'on chante ta justice!
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
L'Éternel est miséricordieux et clément, lent à s'irriter, et riche en grâce.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
L'Éternel est bon envers tous, et sa miséricorde s'étend à toutes ses œuvres.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Éternel, toutes tes œuvres te célèbrent, et tes saints te bénissent;
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
ils disent la gloire de ton empire, et publient ta puissance,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
pour annoncer ta puissance aux enfants des hommes, et le glorieux éclat de ton règne.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Ton régne est un règne de tous les siècles, et ton empire se perpétue d'âge en âge.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
L'Éternel soutient tous ceux qui tombent, et Il redresse ceux qui sont affaissés.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Les yeux de tous s'attendent à toi, et tu leur donnes leur nourriture en son temps.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Tu ouvres ta main, et tu rassasies de faveurs tous les vivants.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
L'Éternel est juste en toutes ses voies, et miséricordieux en tout ce qu'il fait.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
L'Éternel est près de tous ceux qui l'invoquent, de tous ceux qui l'invoquent avec sincérité.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Il accomplit les vœux de ceux qui le craignent, Il entend leur cri, et leur est secourable.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
L'Éternel garde tous ceux qui l'aiment, et Il détruit tous les impies.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Que ma bouche redise la louange de l'Éternel, et que toute chair bénisse son saint nom, éternellement, à jamais!