< Masalimo 145 >

1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Hymne de David. Je veux t’exalter, ô mon Dieu, ô Roi, bénir ton nom jusque dans l’éternité.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Chaque jour je te bénirai, je célébrerai ton nom à jamais.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Grand est l’Eternel et justement glorifié, sa grandeur est sans bornes.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Une génération vante tes œuvres à l’autre, et proclame tes hauts faits.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
La splendeur de ta glorieuse majesté, le détail de tes merveilles, voilà ce que je veux exposer.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Tous célèbrent la puissance de tes prodiges, et moi aussi je veux annoncer ta grandeur.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
Ils ne tarissent pas sur la gloire de ta grande bonté, et ils chantent ta justice.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Clément et miséricordieux est l’Eternel, tardif à la colère et abondant en grâce.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
L’Eternel est bon pour tous, sa pitié s’étend à toutes ses créatures.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Toutes tes œuvres te louent, Seigneur; et tes fidèles adorateurs te bénissent.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
Ils célèbrent l’honneur de ta royauté, et disent ta puissance,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
pour faire connaître aux fils de l’homme tes hauts faits et l’éclat glorieux de ton règne.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Ta royauté remplit toute l’éternité, et ta domination se prolonge d’âge en âge.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
L’Eternel soutient tous ceux qui tombent, et redresse ceux qui sont courbés.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Tous les yeux se tournent avec espoir vers toi, et, toi, tu leur donnes leur subsistance en temps voulu.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Tu ouvres la main et rassasies avec bienveillance tout être vivant.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
L’Eternel est juste en toutes ses voies, et généreux en tous ses actes.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
L’Eternel est proche de tous ceux qui l’invoquent, de tous ceux qui l’appellent avec sincérité.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Il accomplit les désirs de ses fidèles, entend leurs supplications et leur porte secours.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
L’Eternel protège tous ceux qui l’aiment, mais il anéantit tous les impies.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Que ma bouche dise les louanges de l’Eternel, et que toute créature bénisse son saint nom à jamais!

< Masalimo 145 >