< Masalimo 145 >

1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
I will extol you, my God, O king; and I will bless your name for ever and ever.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Every day will I bless you; and I will praise your name for ever and ever.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Great is the LORD, and greatly to be praised; and his greatness is unsearchable.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
One generation shall praise your works to another, and shall declare your mighty acts.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
I will speak of the glorious honour of your majesty, and of your wondrous works.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
And men shall speak of the might of your terrible acts: and I will declare your greatness.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
They shall abundantly utter the memory of your great goodness, and shall sing of your righteousness.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
The LORD is gracious, and full of compassion; slow to anger, and of great mercy.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
The LORD is good to all: and his tender mercies are over all his works.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
All your works shall praise you, O LORD; and your saints shall bless you.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
They shall speak of the glory of your kingdom, and talk of your power;
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
To make known to the sons of men his mighty acts, and the glorious majesty of his kingdom.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Your kingdom is an everlasting kingdom, and your dominion endures throughout all generations.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
The LORD upholds all that fall, and raises up all those that be bowed down.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
The eyes of all wait upon you; and you give them their food in due season.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
You open your hand, and satisfy the desire of every living thing.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
The LORD is righteous in all his ways, and holy in all his works.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
The LORD is nigh unto all them that call upon him, to all that call upon him in truth.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
He will fulfill the desire of them that fear him: he also will hear their cry, and will save them.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
The LORD perserves all them that love him: but all the wicked will he destroy.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
My mouth shall speak the praise of the LORD: and let all flesh bless his holy name for ever and ever.

< Masalimo 145 >